Edit

About Us

The Lilongwe City Council was established under the Local Government Act No. 42 of 1998 as a body corporate. The Council comprises the Political and Administrative arms which both derive their authority from the Local Government Act of 1998. The Political  arm is led by the Mayor who is an elected councillor. The mayor is in charge of 27 Wards each overseen by an elected Councillor.  In addition, there are four (4) elected Members of Parliament who represent the Lilongwe urban sector. There are also five (5)  ex-official members representing interest groups. The Administrative arm of Lilongwe City Council is led by the Chief Executive Officer who oversees nine (9) technical departments and devolved sectors, including Commerce & Trade, Engineering, Education, Youth & Sports Sector, Parks & Recreation, Health and Social Welfare Services, Planning & Development and Finance.

Contact Info

Kugawana ndi kugulitsana malo a Boma mu Mzinda wa Lilongwe

Kugawana ndi kugulitsana malo a Boma mu Mzinda wa Lilongwe

Khonsolo ya Mzinda wa Lilongwe ikudziwitsa anthu omwe akugawana ndikugulitsana malo mmadera osiyanasiyana mumzindawu kuti kutero ndikuphwanya malamulo a za malo (Land Act 2016) ndiponso a zomangamanga (Physical Planning Act 2016).  Khonsoloyi ikuchenjeza iwo omwe akugulitsana ndi kugawana malo ndiponso kumanga mmalowa popanda chilolezo kuti Khonsolo ya Lilongwe idzachotsa katundu womangira (njerwa, mchenga, miyala ndi zina zotero) ndi kuphwanya zomwe anthu angayambe kumanga m’malowa.  Khonsolo ya mzindawu, idzatengeranso ku bwalo lamlandu iwo womwe akugawa ndi kugulitsa malo a Bomawa.

Khonsolo ya Mzinda wa Lilongwe ikudziwitsa onse omwe akugula ndi kuyamba kumanga mmalo osiyanasiyana kuti Khonsolo ya Lilongwe siyinapatse wina aliyense mphamvu yogulitsa malo mu mzindawu. Khonsoloyi ikupempha onse omwe akugula malo ndikuyamba kumanga mmadera monga ku Nsungwi (Area 25), m’mbali mwa msewu wa Kaunda (kuchokera pa Gulliver kumapita chaku Area 25), Area 43 ndi madera ena mu mzindawu, kuti asiye kutero pakuti ngati apitiliza, akhala akutaya ndalama zawo mmadzi pakuti zomangamanga zonse zidzachotsedwa (kugumulidwa) ndi Khonsolo ya Lilongwe popanda kupatsidwa chipuputa misonzi chilichonse.

Tiyeni tonse tikonde mzinda wathu ndi ndalama zathu popewa kumanga m’malo a misewu, manda, mitsinje ndiponso omwe sitinapatsidwe motsata ndondomeko zoyenera. 

Lilongwe City Council

Subscribe Newsletter

Sign up for our latest news & articles. We won’t give you spam mails.

© 2020 Lilongwe City Council. All Rights Reserved